Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 8:28-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. ndipo analinkubwerera, nalikukhala pa gareta wace, nawerenga mneneri Yesaya.

29. Ndipo Mzimu anati kwa Filipo, Yandikira, nudziphatike ku gareta uyu.

30. Ndipo Filipo anamthamangira, namva iye alikuwerenga Yesaya mneneri, ndipo anati, Kodi muzindikira cimene muwerenga?

31. Koma anati, Ndingathe bwanji, popanda munthu wonditsogolera ine? ndipo anapempha Filipo akwere nakhale naye.

32. Koma palembo pamene analikuwerengapo ndipo.Ngati nkhosa anatengedwa kukaphedwa,Ndi monga mwana wa nkhosa ali du pamaso pa womsenga,Kotero sanatsegula pakamwa pace:

33. M'kucepetsedwa kwace ciweruzo cace cinacotsedwa;Mbadwo wace adzaubukitsa ndani?Cifukwa wacotsedwa kudziko moyo wace.

34. Ndipo mdindoyo anayankha Filipo, nati, Ndikupempha, mneneri anena ici za yani? za yekha, kapena za wina?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 8