Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 8:2-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo anamuika Stefano anthu opembedza, namlira maliro akuru.

3. Ndipo Saulo anapasula Mpingo, nalowa m'nyumba m'nyumba, nakokamo amuna ndi akazi, nawaika m'ndende.

4. Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo.

5. Ndipo Filipo anatsikira ku mudzi wa ku Samarlya, nawalalikira iwo Kristu.

6. Ndipo makamuwo ndi mtima umodzi anasamalira zonenedwa ndi Filipo, pamene anamva, napenya zizindikilo zimene anazicita.

7. Pakuti ambiri a iwo akukhala nayo mizimu yonyansa inawaturukira, yopfuula ndi mau akuru; ndipo ambiri amanjenje, ndi opunduka, anaciritsidwa.

8. Ndipo panakhala cimwemwe cacikuru m'mudzimo.

9. Koma panali munthu dzina lace Simoni amene adacita matsenga m'mudzimo kale, nadabwitsa anthu a Samariya, ndi kunena kuti iye yekha ndiye munthu wamkuru;

10. ameneyo anamsamalira onsewo, kuyambira wamng'ono kufikira wamkuru, ndi kunena, Uyu ndiye mphamvu ya Mulungu, yonenedwa Yaikuru.

11. Ndipo anamsamalira iye, popeza nthawi yaikuru adawadabwitsa iwo ndi matsenga ace.

12. Koma pamene anakhulupirira Filipo wakulalikira Uthenga Wabwinowa Ufumu wa Mulungu ndi dzina la Yesu Kristu, anabatizidwa, amuna ndi akazi.

13. Ndipo Simoni mwini wace anakhulupiranso: ndipo m'mene anabatizidwa, anakhalira ndi Filipo; ndipo pakuona zizindikilo ndi mphamvu zazikuru zirikucitika, anadabwa.

14. Koma pamene atumwi a ku Yerusalemu anamva kuti Samariya adalandira mau a Mulungu, anawatumizira Petro ndi Yohane;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 8