Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 8:15-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. amenewo, m'mene adatsikirako, anawapempherera, kuti alandire Mzimu Woyera:

16. pakuti kufikira pamenepo nkuti asanagwe pa wina mmodzi wa iwo; koma anangobatizidwam'dzina la Ambuye Yesu.

17. Pamenepo anaika manja pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.

18. Koma pakuona Simoni kuti mwa kuika manja a atumwi anapatsidwa Mzimu Woyera, anawatengera ndalama,

19. nanena, Ndipatseni inenso ulamuliro umene, kuti amene ali yense ndikaika manja pa iye, alandire Mzimu Woyera.

20. Koma Petro anati kwa iye, Ndalama yako itayike nawe, cifukwa unalingirira kulandira mphatso ya Mulungu ndi ndalama.

21. Ulibe gawo kapena colandira ndi mau awa; pakuti mtima wako suli wolunjika pamaso pa Mulungu.

22. Cifukwa: cace lapa coipa calm ici, pemphera Ambuye, kuti kapena akukhululukire iwe colingiriraca mtima wako.

23. Pakuti ndiona kuti wagwidwa ndi ndulu yowawa ndi nsinga ya cosalungama.

24. Ndipo Simoni anayankha nati, Mundipempherere ine kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.

25. Pamenepo iwo, atatha kucita umboni ndi kulankhula mau a Ambuye, anabwerakunkaku Yerusalemu, nalalikira Uthenga Wabwi no ku midzi yambirl ya Asamariya.

26. Koma mngelo wa Ambuye analankhula ndi Filipo, nanena, Nyamuka, nupite mbali ya kumwela, kutsata njira yotsika kucokera ku Yerusalemu kunka ku Gaza; ndiyo ya cipululu.

27. Ndipo ananyamuka napita; ndipo taona munthu wa ku Aitiopiya, mdindo wamphamvu wa Kandake, mfumu yaikazi ya Aaitiopiya, ndiye wakusunga cuma cace conse, amene anadza ku Yerusalemu kudzapemphera;

28. ndipo analinkubwerera, nalikukhala pa gareta wace, nawerenga mneneri Yesaya.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 8