Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 7:32-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. 5 akuti, Ine ndine Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, ndi wa Isake, ndi wa Yakobo. Ndipo Mose ananthunthumira, osalimbika mtima kupenyetsako.

33. 6 Ndipo Ambuye anati kwa iye, Masula nsapato ku mapazi ako; pakuti pa malo amene upondapo mpopatulika.

34. 7 Kuona ndaona coipidwa naco anthu anga ali m'Aigupto, ndipo a amva kubuula kwao; ndipo ndatsika kuwalanditsa; ndipo tsopano tiye kuno, ndikutume ku Aigupto

35. Mose uyu amene anamkana, ndi kuti, Wakuika iwe ndani mkuru ndi woweruza? ameneyo Mulungu anamtuma akhale mkuru, ndi mombolo, ndi dzanja la mngelo womuonekera pacitsamba.

36. Ameneyo anawatsogolera, naturuka nao 8 atacita zozizwa ndi zizindikilo m'Aigupto, ndi m'Nyanja Yofiira, ndi m'cipululu zaka makumi anai.

37. Uyu ndi Mose uja adati kwa ana a Israyeli, 9 Mulungu adzakuutsirani Mneneri wa mwa abale anu, monga ine.

38. 10 Uyu ndiye amene anali mu Mpingo m'cipululu pamodzi ndi mngelo wakulankhula naye m'phiri la Sina, ndi makolo athu: amene analandira maneno amoyo akutipatsa ife;

39. amene makolo athu sanafuna kumvera iye, koma anamkankha acoke, nabwerera m'mbuyo mumtima mwao ku Aigupto,

40. 11 nati ndi Aroni, Tipangireni milungu yotitsogoleraife; pakuti Mose uja, amene anatiturutsa m'Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 7