Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 7:26-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo m'mawa mwace anawaonekera alikulimbana ndeu, ndipo anati awateteze, ayanjanenso, nati, Amuna inu, muli abale; mucitirana coipa bwanji?

27. koma iye wakumcitira mnzace coipa anamkankha, nati, Wakuika iwe ndani mkulu ndi wotiweruzira?

28. 1 Kodi ufuna kundipha ine, monga muja unapha M-aigupto dzulo?

29. 2 Ndipo Mose anathawa pa mau awa, nakhala mlendo m'dziko la Midyani; kumeneko anabala ana amuna awiri.

30. Ndipo 3 zitapita zaka makumi anai, anamuonekera mngelo m'cipululu ca Sina, m'lawi la mota wa m'citsamba.

31. 4 Koma Mose pakuona, anazizwa pa coonekaco; ndipo pakuyandikira iye kukaona, kunadza mau a Ambuye,

32. 5 akuti, Ine ndine Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, ndi wa Isake, ndi wa Yakobo. Ndipo Mose ananthunthumira, osalimbika mtima kupenyetsako.

33. 6 Ndipo Ambuye anati kwa iye, Masula nsapato ku mapazi ako; pakuti pa malo amene upondapo mpopatulika.

34. 7 Kuona ndaona coipidwa naco anthu anga ali m'Aigupto, ndipo a amva kubuula kwao; ndipo ndatsika kuwalanditsa; ndipo tsopano tiye kuno, ndikutume ku Aigupto

35. Mose uyu amene anamkana, ndi kuti, Wakuika iwe ndani mkuru ndi woweruza? ameneyo Mulungu anamtuma akhale mkuru, ndi mombolo, ndi dzanja la mngelo womuonekera pacitsamba.

36. Ameneyo anawatsogolera, naturuka nao 8 atacita zozizwa ndi zizindikilo m'Aigupto, ndi m'Nyanja Yofiira, ndi m'cipululu zaka makumi anai.

37. Uyu ndi Mose uja adati kwa ana a Israyeli, 9 Mulungu adzakuutsirani Mneneri wa mwa abale anu, monga ine.

38. 10 Uyu ndiye amene anali mu Mpingo m'cipululu pamodzi ndi mngelo wakulankhula naye m'phiri la Sina, ndi makolo athu: amene analandira maneno amoyo akutipatsa ife;

39. amene makolo athu sanafuna kumvera iye, koma anamkankha acoke, nabwerera m'mbuyo mumtima mwao ku Aigupto,

40. 11 nati ndi Aroni, Tipangireni milungu yotitsogoleraife; pakuti Mose uja, amene anatiturutsa m'Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

41. Ndipo 12 anapanga mwana wa ng'ombe masiku omwewo, nabwera nayo nsembe kwa fanolo, nasekerera ndi nchito za manja ao.

42. Koma 13 Mulungu anatembenuka, nawapereka iwo atumikire gulu la kumwamba; monga kwalembedwa m'buku laaneneri,14 Kodi mwapereka kwa Ine nyama zophedwa ndi nsembeZaka makumi anai m'cipululu, nyumba ya Israyeli inu?

43. 15 Ndipo munatenga cihema ca Moloki,Ndi nyenyezi ya mulungu Refani,Zithunzizo mudazipanga kuzilambira;Ndipo ndidzakutengani kunka nanu m'tsogolo mwace mwa Babulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 7