25. amene mwa Mzimu Woyera, pakamwa pa kholo lathu Davine mtumiki wanu, mudati,Amitundu anasokosera cifukwaciani?Nalingirira zopanda pace anthu?
26. Anadzindandalitsa mafumu a dziko,Ndipo oweruza anasonkhanidwa pamodzi,Kutsutsana ndi Ambuye, ndi Kristu wace.
27. Pakuti zoonadi anasonkhanidwa m'mudzi muno Herode, ndi Pontiyo Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israyeli kumcitira coipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza;