Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 4:22-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pakuti anali wa zaka zace zoposa makumi anai munthuyo, amene cizindikilo ici cakumciritsa cidacitidwa kwa iye.

23. Ndipo m'mene anamasulidwa, anadza kwa anzao a iwo okha, nawauza ziri zonse oweruza ndi akulu adanena nao.

24. Ndipo m'mene adamva, anakweza mau kwa Mulungu ndi mtima umodzi, nati, Mfumu, Inu ndinu wolenga thambo la kumwamba ndi dziko, ndi nyanja, ndi zonse ziri m'menemo;

25. amene mwa Mzimu Woyera, pakamwa pa kholo lathu Davine mtumiki wanu, mudati,Amitundu anasokosera cifukwaciani?Nalingirira zopanda pace anthu?

26. Anadzindandalitsa mafumu a dziko,Ndipo oweruza anasonkhanidwa pamodzi,Kutsutsana ndi Ambuye, ndi Kristu wace.

27. Pakuti zoonadi anasonkhanidwa m'mudzi muno Herode, ndi Pontiyo Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israyeli kumcitira coipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 4