Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 28:5-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Koma anakutumulira ciromboco kumoto, osamva kupweteka.

6. Koma anayesa kuti adzatupa, kapena mwini wace kugwa kufa pomwepo; koma m'mene adalindira nthawitu, naona kuti sikunampweteka, anapindula, nati, Ndiye Mulungu.

7. Koma pafupt pamenepo panali minda, mwini wace ndiye mkulu cisumbuco, dzina lace Popliyo; amene anatilandira ife, naticereza okoma masiku atatu.

8. Ndipo kunatero kuti atate wace wa Popliyo anagona wodwala nthenda ya malungo ndi kamwazi. Kwa iyeyu Paulo analowa, napemphera, naika manja pa iye, namciritsa.

9. Ndipo patacitika ici, enanso a m'cisumbu, okhala nazo nthenda, anadza, naciritsidwa;

10. amenenso anaticitira ulemu wambiri; ndipo pocoka ife anatiikira zotisowa.

11. Ndipo itapita miyezi itatu tinayenda m'ngalawa ya ku Alesandriya, idagonera nyengo ya cisanu kucisumbuko, cizindikilo cace, Ana-a-mapasa.

12. Ndipo pamene tinakoceza ku Surakusa, tinatsotsako masiku atatu.

13. Ndipo pocokapo tinapaza ntifika ku Regio; ndipo litapita tsiku limodzi unayamba mwela, ndipo m'mawa mwace tinafika ku Potiyolo:

14. pamenepo tinakomana ndi abale, amene anatiumirira tikhale nao masiku asanu ndi awiri; ndipo potero tinafika ku Roma.

15. Kucokera kumeneko abalewo, pakumva za ife, anadza kukomana nafe ku Bwalo la Apiyo, ndi ku Nyumba za Alendo Zitatu; ndipo pamene Paulo anawaona, anayamika Mulungu, nalimbika mtima.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 28