Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 28:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Koma pakukanapo Ayuda, ndinafulumidwa mtima kuturukira kwa Kaisara; si kunena kuti ndinali nako kanthu kakunenera mtundu wanga.

20. Cifukwa ca ici tsono ndinakupemphani inu mundione ndi kulankhula nane; pakuti cifukwa ca ciyembekezo ca Israyeli ndamangidwa ndi unyolo uwu.

21. Ndipo anati kwa iye, Ife sitinalandira akalata onena za inu ocokera ku Yudeya, kapena sanadza kuno wina wa abale ndi kutiuza kapena kulankhula kanthu koipa ka inu.

22. Koma tifuna kumva mutiuze muganiza ciani; pakuti za mpatuko uwu, tidziwa kuti aunenera ponse ponse.

23. Ndipo pamene adampangira tsiku, anadza ku nyumba yace anthu ambiri; amenewo anawafotokozera, ndikucitira umboni Ufumu wa Mulungu, ndi kuwakopa za Yesu, zocokera m'cilamulo ca Mose ndi mwa aneneri, kuyambira mamawa kufikira madzulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 28