Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 28:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo kunali, atapita masiku atatu, anaitana akulu a Ayuda asonkhane; ndipo atasonkhana, ananena nao, Ine, amuna, abale, ndingakhale sindinacita kanthu kakuipsa anthu, kapena miyambo ya makolo, anandipereka wam'nsinga kucokera ku Yerusalemu ku manja a Aroma;

18. ndiwo, atandifunsafunsa ine anafuna kundimasula, popeza panalibe cifukwa ca kundiphera.

19. Koma pakukanapo Ayuda, ndinafulumidwa mtima kuturukira kwa Kaisara; si kunena kuti ndinali nako kanthu kakunenera mtundu wanga.

20. Cifukwa ca ici tsono ndinakupemphani inu mundione ndi kulankhula nane; pakuti cifukwa ca ciyembekezo ca Israyeli ndamangidwa ndi unyolo uwu.

21. Ndipo anati kwa iye, Ife sitinalandira akalata onena za inu ocokera ku Yudeya, kapena sanadza kuno wina wa abale ndi kutiuza kapena kulankhula kanthu koipa ka inu.

22. Koma tifuna kumva mutiuze muganiza ciani; pakuti za mpatuko uwu, tidziwa kuti aunenera ponse ponse.

23. Ndipo pamene adampangira tsiku, anadza ku nyumba yace anthu ambiri; amenewo anawafotokozera, ndikucitira umboni Ufumu wa Mulungu, ndi kuwakopa za Yesu, zocokera m'cilamulo ca Mose ndi mwa aneneri, kuyambira mamawa kufikira madzulo.

24. Ndipo ena anamvera zonenedwazo, koma ena sanamvera.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 28