Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 25:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. nampempha kuti mlandu wace wa Paulo uipe, kuti amuitane iye adze ku Yerusalemu; iwo amcitira cifwamba kuti amuphe panjira.

4. Pamenepo Festo anayankha, kuti Paulo asungike ku Kaisareya, ndi kuti iye mwini adzapitako posacedwa.

5. Cifukwa cace, ati, iwo amene akhoza mwa inu amuke nane potsikirako, ndipo ngati kuli kanthu kosayenera mwa munthuyo amnenere iye.

6. Ndipo m'mene adatsotsa mwa iwo masiku asanu ndi atatu kapena khumi okha anatsikiraku Kaisareya; ndipo m'mawa mwace anakhala pa mpando waciweruziro, nalamulira kuti atenge Paulo.

7. Ndipo m'mene anafika iye, Ayuda adatsikawo ku Yerusalemu anaimirira pomzinga iye, namnenera zifukwa zambiri ndi zazikuru, zimene sanakhoza kuzitsimikiza;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 25