Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 25:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. koma anali nao mafunso ena otsutsana naye a cipembedzero ca iwo okha, ndi mafunso a wina Yesu, amene adafa, amene Paulo anati kuti ali ndi moyo.

20. Ndipo ine posinkhasinkha za mafunso awa ndinamfunsa ngati afuna kupita ku Yerusalemu, ndi kuweruzidwa komweko za izi.

21. Koma pakunena Paulo ndi kuti, asungidwe, akaturukire kwa Augusto, ndinaweruza asungidwe iye kufikira ndikamtumiza kwa Kaisara.

22. Ndipo Agripa anati kwa Festo, Ndifuna nanenso ndimve munthuyo. Anati, Mawa mudzamva iye.

23. M'mawa mwace tsono, atafika Agripa ndi Bemike ndi cifumu cacikuru, ndipo atalowa momvera milandu, pamodzi ndi akapitao akuru, ndi amuna omveka a mudziwo, ndipo pakulamulira Festo, anadza naye Paulo.

24. Ndipo Festo anati, Mfumu Agripa, ndi amuna inu nonse muli nafe pano pamodzi, muona uyu, amene unyinji wonse wa Ayuda anandiuza za iye, ku Yerusalemu ndi kunonso, ndi kupfuula kuti sayeneranso kukhala ndi moyo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 25