Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 25:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Festo m'mene analowa dziko lace, ndipo atapita masiku atatu, anakwera kunka ku Yerusalemu kucokera ku Kaisareya.

2. Ndipo ansembe akulu ndi akulu a Ayuda ananenera Paulo kwa iye; ndipo iwo anamdandaulira,

3. nampempha kuti mlandu wace wa Paulo uipe, kuti amuitane iye adze ku Yerusalemu; iwo amcitira cifwamba kuti amuphe panjira.

4. Pamenepo Festo anayankha, kuti Paulo asungike ku Kaisareya, ndi kuti iye mwini adzapitako posacedwa.

5. Cifukwa cace, ati, iwo amene akhoza mwa inu amuke nane potsikirako, ndipo ngati kuli kanthu kosayenera mwa munthuyo amnenere iye.

6. Ndipo m'mene adatsotsa mwa iwo masiku asanu ndi atatu kapena khumi okha anatsikiraku Kaisareya; ndipo m'mawa mwace anakhala pa mpando waciweruziro, nalamulira kuti atenge Paulo.

7. Ndipo m'mene anafika iye, Ayuda adatsikawo ku Yerusalemu anaimirira pomzinga iye, namnenera zifukwa zambiri ndi zazikuru, zimene sanakhoza kuzitsimikiza;

8. koma Paulo podzikanira ananena, Sindinacimwa kanthu kapena pacilamulo, kapena paKacisi, kapena pa Kaisara.

9. Kama Festo pofuna kuyesedwa wacisomo ndi Ayuda, anayankha kwa Paulo, nati, Kodi ufuna kukwera kunka ku Yerusalemu, ndi kuweruzidwa ndi ine pomwepo kunena za zinthu izi?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 25