Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 23:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Paulo, popenyetsetsa a m'bwalo la akuru anati, Amuna, abale, ndakhala ine pamaso pa Mulungu ndi cikumbu mtima cokoma conse kufikira lero lomwe.

2. Ndipo mkulu wa ansembe Hananiya analamulira akuimirirako ampande pakamwa pace.

3. Pamenepo Paulo anati kwa iye, Mulungu adzakupanda iwe, khoma loyeretsedwa iwe; ndipo kodi ukhala iwe wakundiweruza mlandu monga mwa cilamulo, ndipo ulamulira andipande ine posanga cilamulo?

4. Ndipo iwo akuimirirako anati, Ulalatira kodi mkulu wa ansembe wa Mulungu?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 23