Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 22:3-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ine ndine munthu Myuda, wobadwa m'Tariso wa Kilikiya, koma ndaleredwa m'mzinda muno, pa mapazi a Gamaliyeli, wolangizidwa monga mwa citsatidwe ceni ceni ca cilamulo ca makolo athu, ndipo ndinali wacangu, colinga kwa Mulungu, monga muli inu nonse lero;

4. ndipo ndinalondalonda Njira iyi kufikira imfa, ndi kumanga ndi kupereka kundende amuna ndi akazi.

5. Monganso mkulu wa ansembe andicitira umboni, ndi bwalo lonse la akuru; kwa iwo amenenso ndinalandira akalata kunka nao kwa abale, ndipo ndinapita ku Damasiko, kuti ndikatenge iwonso akukhala kumeneko kudza nao omangidwa ku Yerusalemu, kuti alangidwe.

6. Ndipo kunali, pakupita ine ndi kuyandikira ku Damasiko, monga usana, mwadzidzidzi kunandiwalira pondizungulira ine kuunika kwakukuru kocokera kumwamba.

7. Ndipo ndinagwapansitu, ndipondinamva mau akunena nane, Saulo, Saulo, undilonda-londeranii Ine?

8. Ndipo ndinayankha, Ndinu yani Mbuye? Ndipo anati kwa Ine, Ndine Yesu wa ku Nazarete, amene umlondalonda.

9. Ndipo iwo akukhala nane anaonadi kuunika, koma sanamva mau akulankhula nane.

10. Ndipo ndinati, ndidzacita ciani, Ambuye? Ndipo Ambuye anati kwa ine, Taukavpita ku Damasiko; kumeneko adzakufotokozera zonse zoikika kwa iwe uzicite.

11. Ndipo popeza sindinapenya, cifukwa ca ulemerero wa kuunikako, anandigwira dzanja iwo amene anali ndi ine, ndipo ndinafika ku Damasiko.

12. Ndipo munthu dzina lace Hananiya, ndiye munthu wopembedza monga mwa cilamulo, amene amcitira umboni wabwino Ayuda onse akukhalako,

13. anadza kwa ine, ndipo poimirirapo anati kwa ine, Saulo, mbale, penyanso. Ndipo ine, ora lomweli ndinampenya.

14. Ndipo anati, Mulungu wa makolo athu anakusankhiratu udziwe cifuniro cace, nuone Wolungamayo, numve mau oturuka m'kamwa mwace.

15. Ndipo udzamkhalira iye mboni kwa anthu onse, za izo udaziona ndi kuzimva.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 22