Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 22:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Amuna, abale, ndi atate, mverani codzikanira canga tsopano, ca kwa inu.

2. Ndipo pakumva kuti analankhula nao m'cinenedwe ca Cihebri, anaposa kukhala cete; ndipo anati:

3. ine ndine munthu Myuda, wobadwa m'Tariso wa Kilikiya, koma ndaleredwa m'mzinda muno, pa mapazi a Gamaliyeli, wolangizidwa monga mwa citsatidwe ceni ceni ca cilamulo ca makolo athu, ndipo ndinali wacangu, colinga kwa Mulungu, monga muli inu nonse lero;

4. ndipo ndinalondalonda Njira iyi kufikira imfa, ndi kumanga ndi kupereka kundende amuna ndi akazi.

5. Monganso mkulu wa ansembe andicitira umboni, ndi bwalo lonse la akuru; kwa iwo amenenso ndinalandira akalata kunka nao kwa abale, ndipo ndinapita ku Damasiko, kuti ndikatenge iwonso akukhala kumeneko kudza nao omangidwa ku Yerusalemu, kuti alangidwe.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 22