Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 21:29-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Pakuti adaona Trofimo wa ku Efeso kale pamodzi ndi iye mumzinda; ameneyo anayesa kuti Paulo anamtenga nalowa naye kuKacisi.

30. Ndipo mudzi wonse unasokonezeka, ndipo anthu anathamangira pamodzi; nagwira Paulo namkoka kumturutsa m'Kacisi; ndipo pomwepo pamakomo panatsekedwa.

31. Ndipo m'mene anafuna kumupha iye, wina anamuuza kapitao wamkuru wa gululo kuti m'Yerusalemumonse muli pinngu-piringu,

32. Ndipo posacedwa iye anatenga asilikari ndi akenturiyo, nathamanga, nawatsikira; ndipo iwowa, pakuona kapitao wamkuru ndi asilikari, analeka kumpanda Paulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 21