15. Ndipo atapita masiku awa tinakonza akatundu athu, ntikwera ku Yerusalemu.
16. Ndipo anamuka nafenso ena a ophunzira a ku Kaisareya, natenganso wina Mnaso wa ku Kupro, wophunzira wakale, amene adzaticereza.
17. Ndipo pofika ife ku Yerusalemu, abale anatilandira mokondwera.
18. Ndipo m'mawa mwace Paulo analowa nafe kwa Yakobo; ndi akulu onse anali pomwepo.
19. Ndipo atawalankhula iwo, anawafotokozera cimodzi cimodzi zimene Mulungu anacita kwa amitundu mwa utumiki wace.
20. Ndipo pamene anazimva, analemekeza Mulungu; nati kwa iye, Uona, mbale, kuti ambirimbiri mwa Ayuda akhulupira; ndipo ali naco cangu onsewa, ca pa cilamulo;
21. ndipo anamva za iwe, kuti uphunzitsa Ayuda onse a ku amitundu apatukane naye Mose, ndi kuti asadule ana ao, kapena asayende monga mwa miyambo.
22. Nciani tsono? adzamva ndithu kuti wafika.
23. Cifukwa cace ucite ici tikuuza iwe; tiri nao amuna anai amene anawinda;
24. amenewa uwatenge nudziyeretse nao pamodzi, nuwalipirire, kati amete mutu; ndipo adzadziwa onse kuti zomveka za iwe nzacabe, koma kuti iwe wekhaoso uyenda molunjika, nusunga cilamulo.