Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 21:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo pokhalapo masiku ambiri, anatsika ku Yudeya mneneri, dzina lace Agabo.

11. Ndipo anadza kwa ife natenga lamba la Paulo, nadzimanga yekha manja ndi mapazi, nati, Atero Mzimu Woyera, Munthu mwini lamba ili, adzammanga kotero Ayuda a m'Yerusalemu, nadzampereka m'manja a amitundu.

12. Koma pamene tinamva izi tinamdandaulira ife ndi iwo a komweko, asakwere iye kunka ku Yerusalemu.

13. Pamenepo Paulo anayankha, Mucitanji, polira ndi kundiswera mtima? pakuti ndakonzeka Ine si kumangidwa kokha, komatunso kufera ku Yerusalemu cifukwa ca dzina la Ambuye Yesu.

14. Ndipo pokana iye kukopeka, tinaleka, ndi kuti, Kufuna kwa Ambuye kucitidwe.

15. Ndipo atapita masiku awa tinakonza akatundu athu, ntikwera ku Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 21