1. Ndipo kunali, titalekana nao ndi kukankha ngalawa, tinadza molunjika ku Ko, ndi m'mawa mwace ku Rode, ndipo pocokerapo ku Patara;
2. ndipo m'mene tinapeza ngalawa Yakuoloka kunka ku Foinike, tinalowamo, ndi kupita nayo.
3. Ndipo pamene tinafika popenyana ndi Kupro, tinacisiya kulamanzere, ntinapita ku Suriya; ndipo tinakoceza ku Turo; pakuti pamenepo ngalawainafuna kutula akatundu ace.
4. Ndipo m'mene tinapeza ophunzira, tinakhalako masikuasanu ndi awiri; ndipo iwowa ananena ndi Paulo mwa Mzimu, kuti asakwere ku Yerusalemu.
5. Ndipo kunali pamene tidatsiriza masikuwa, tidacoka ndi kunka ulendo wathu; ndipo iwo onse, akazi ndi ana anatiperekeza kufikira kuturuka m'mudzi; ndipo pogwadira pa mcenga wa kunyanja, tinapemphera,
6. ndi kulawirana; ndipo tinalowa m'ngalawa, koma iwo anabwera kwao.