Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 20:12-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo anadza naye mnyamata ali wamoyo, natonthozedwa kwakukuru.

13. Koma ife tinatsogolera kunka kungalawa, ndipo tinapita ku Aso, pamenepo tinati timlandire Paulo; pakuti anatipangira comweco, koma anati ayenda pamtunda yekha.

14. Ndipo pamene anakomana ndi ife ku Aso, tinamlandira, ndipo tinafika ku Mitilene.

15. Ndipo m'mene tidacokerapo, m'mawa mwace tinafika pandunjipa Kiyo; ndi m'mawa mwace tinangokoceza ku Samo, ndi m'mawa mwace tinafika ku Mileto.

16. Pakuti Paulo adatsimikiza mtima apitirire pa Efeso, angataye nthawi m'Asiya; pakuti anafulumira, ngati kutheka, akhale ku Yerusalemu tsiku la Pentekoste.

17. Ndipo pokhala ku Mileto anatuma ku Efeso, naitana akulu a Mpingo.

18. Ndipo pamene anafika kuli iye, anati kwa iwo,Mudziwa inu kuyambira tsiku loyamba ndinafika ku Asiya, makhalidwe anga pamodzi ndi inu nthawi yonse,

19. wotumikira Ambuye ndi kudzicepetsa konse ndi misozi, ndi mayesero anandigwera ndi ziwembu za Ayuda;

20. kuti sindinakubisirani zinthu zopindulira, osazilalikira kwa inu, ndi kukuphunzitsani inu pabwalo ndi m'nyumba m'nyumba,

21. ndi kucitira umboni Ayuda ndi Ahelene wa kutembenuza mtima kulinga kwa Mulungu, ndi cikhulupiriro colinga kwa Ambuye wathu Yesu Kristu.

22. Ndipo, taonani, ndipita ku Yerusalemu womangidwa mumzimu, wosadziwa zimene zidza'ndigwera ine kumeneko;

23. koma kuti Mzimu Woyera andicitira umboni m'midzi yonse, ndi kunena kuti nsinga ndi zisautso zindilindira.

24. Komatu sindiuyesa kanthu moyo, wanga, kuti uli wa mtengo wace kwa ine ndekha; kotero kuti ndikatsirize njira yanga, ndi utumiki ndinaulandira kwa Ambuye Yesu, kucitira umboni Uthenga Wabwino wa cisomo ca Mulungu.

25. Ndipo tsopano, taonani, ndidziwa ine kuti inu nonse amene ndinapitapita mwa inu kulalikira ufumuwo, simudzaonanso nkhope yanga.

26. Cifukwa cace ndikucitirani umboni lero lomwe, kuti ndiribe kanthu ndi mwazi wa anthu onse.

27. Pakuti sindinakubisirani pakukulalikirani uphungu wonse wa Mulungu.

28. Tadzicenjerani nokha, ndi gulu lonse, pamenepo Mzimu Woyera anakuikani oyang'anira, kuti muwete Eklesia wa Mulungu, umene anaugula ndi mwazi wa iye yekha.

29. Ndidziwa ine kuti, nditacoka ine, adzalowa mimbulu yosautsa, yosalekerera gululo;

30. ndipo mwa inu nokha adzauka anthu, olankhula zokhotakhota, kupatutsa ophunzira awatsate.

31. Cifukwa cace dikirani, nimukumbukile kuti zaka zitatu sindinaleka usiku ndi usana kucenjeza yense wa inu ndi misozi.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 20