Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 19:34-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Koma pozindikira kuti ali Myuda, kunali mau amodzi a kwa onse akupfuula monga maora awiri, Wamkuru ndi Artemi wa Aefeso.

35. Ndipo pamene mlembi adatontholetsa khamulo, anati, Amuna a Efeso inu, munthuyu ndani wosadziwa kuti mudzi wa Aefeso ndiwo wosungira kacisi wa Artemi wamkuru, ndi fano Iidacokera kwa Zeu?

36. Popeza tsono izi sizikanika, muyenera inu kukhala cete, ndi kusacita kanthu kaliuma.

37. Pakuti mwatenga anthu awa, osakhala olanda za m'kacisi, kapena ocitira mulungu wathu mwano.

38. Ngati tsono Demetriyo ndi amisiri okhala naye, ali ndi mlandu ndi munthu, mabwalo a mirandu alipo, ndi ziwanga ziripo; anenezane.

39. Koma ngati mufuna kanthu ka zinthu zina, kadzakonzeka m'msonkhano wolamulidwa.

40. Pakutinso palipo potiopsya kuti adzatineneza za cipolowe ca lero; popeza palibe cifukwa ca kufotokozera za cipiringu cimene.

41. Ndipo pamene ananena izi, anamasula msonkhano.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 19