Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 19:21-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo zitatha izi, Paulo anatsimikiza mu mzimu wace, atapita pa Makedoniya ndi Akaya, kunka ku Yerusalemu, kuti, Nditamuka komweko ndiyenera kuonanso ku Roma.

22. Pamene anatuma ku Makedoniya awiri a iwo anamtumikira, Timoteo ndi Erasto, iye mwini anakhalabe nthawi m'Asiya.

23. Nthawi yomweyo kunali phokoso lambiri kunena za Njirayo.

24. Pakuti munthu wina dzina lace Demetriyo wosula siliva, amene anapanga tiakacisi tasiliva ta Artemi, anaonetsera amisiri phindu lambiri;

25. amenewo iye anawasonkhanitsa pamodzi ndi amisiri a nchito yomweyo, nati, Amuna inu, mudziwa kuti ndi malonda awa ife tipeza cuma cathu.

26. Ndipo muona ndi kumva, kuti si pa Efeso pokha, koma monga pa Asiya ponse, Paulo uyu akopa ndi kutembenutsa anthu ambiri, ndi kuti, Si milungu iyi imene ipangidwa ndi manja:

27. ndipo tiopa ife kuti nchito yathuyi idzayamba kunyonyosoka; komanso kuti kacisi wa mlungu wamkazi Artemi adzayamba kuyesedwa wacabe; ndiponso kuti iye adzayamba kutsitsidwa ku ukulu wace, iye amene a m'Asiya onse, ndi onse a m'dziko lokhalamo anthu, ampembedza.

28. Ndipo pamene anamva, anadzala ndi mkwiyo, napfuula, nati, Wamkuru ndi Artemi wa ku Efeso,

29. Ndipo m'mudzi monse munacita piringu-piringu, nathamangira onse pamodzi ku bwalo losewera, atagwira Gayo ndi Aristarko, anthu a ku Makedoniya, alendo anzace a Paulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 19