Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 18:15-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. koma akakhala mafunso a mau ndi maina ndi cilamulo canu; muyang'ane inu nokha; sindifuna kuweruza zimenezi.

16. Ndipo anawapitikitsa pa mpando wa ciweruziro.

17. Ndipo anamgwira Sostene, mkuru wa sunagoge, nampanda ku mpando wa ciweruziro. Ndipo Galiyo sanasamalira zimenezi.

18. Paulo atakhala cikhalire masiku ambiri, anatsazika abale, nacoka pamenepo, napita m'ngalawa ku Suriya, pamodzi naye Priskila ndi Akula; popeza anameta mutu wace m'Kenkreya; pakuti adawinda.

19. Ndipo iwo anafika ku Efeso, ndipo iye analekana nao pamenepo: koma iye yekha analowa m'sunagoge, natsutsana ndi Ayuda.

20. Pamene iwo anamfunsa iye kuti akhale nthawi yina yoenjezerapo, sanabvomereza;

21. koma anawatsazika, nati, Akafuna Mulungu, ndidzabwera kwa inu; ndipo anacoka ku Efeso m'ngalawa.

22. Ndipo pamene anakoceza pa Kaisareya, anakwera nalankhulana nao Mpingo, natsikira ku Antiokeya.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 18