Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 16:22-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo linagumukira iwo khamulo; ndipo oweruza anawang'ambira maraya ao; nalamulira kuti awakwapule.

23. Pamene anawaonetsa mikwingwirima yambiri, anawaika m'ndende, nauza mdindo kuti awasunge bwino.

24. Pakumva iye kulamulira kotero anawaika m'cipinda ca m'kati, namangitsa mapazi ao m'zigologolo.

25. Koma ngati pakati pa usiku, Paulo ndi Sila analinkupemphera, nayimbira Mulungu nyimbo, ndipo a m'ndendemo analinkuwamva;

26. ndipo mwadzidzidzi panali cibvomezi cacikuru, cotero kuti maziko a ndende anagwedezeka: pomwepo pamakomo ponse panatseguka; ndi maunyolo a onse anamasuka.

27. Pamene anautsidwa kutulo mdindoyo, anaona kuti pa makomo a ndende panatseguka, ndipo anasolola lupanga lace, nati adziphe yekha, poyesa kuti am'ndende adathawa.

28. Koma Paulo anapfuula ndi mau akuru, nati, Usadzipweteka wekha; tonse tiri muno.

29. Ndipo mdindo anaitanitsa nyali, natumphira m'kati, alinkunthunthunrlra ndi mantha, nagwa pamaso pa Paulo ndi Sila,

30. nawaturutsira iwo kunja, nati, Ambuye, ndicitenji kuti ndipulumuke?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 16