Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 16:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anafikanso ku Derbe ndi Lustra; ndipo taonani, panali wophunzira wina pamenepo, dzina lace Timoteo, amace ndiye Myuda wokhulupira; koma atate wace ndiye Mhelene.

2. Ameneyo anamcitira umboni wabwino abale a ku Lustra ndi Ikoniyo.

3. Iyeyo Paulo anafuna kuti amuke naye, ndipo anamtenga, namdula, cifukwa ca Ayuda amene anakhala m'maikomo; pakuti onse anadziwa kuti atate wace anali Mhelene.

4. Pamene anapita kupyola pamidzi, anapereka kwa iwo malamulo awasunge, amene analamulira atumwi ndi akuru a pa Yerusalemu.

5. Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao tsiku ndi tsiku.

6. Ndipo anapita pa dziko la Frugiya ndi Galatiya, atawaletsa Mzimu Woyera kuti asalalikire mau m'Asiya; pamene anafika kundunji kwa Musiya,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 16