Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 15:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo iwo anaperekezedwa ndi Mpingo, napita pa Foinike ndi Samariya, nafotokozera cisanduliko ca amitundu; nakondweretsa kwambiri abale onse.

4. Pamene anafika ku Yerusalemu, analandiridwa ndi Mpingo, ndi atumwi ndi akuru, ndipo anabwerezanso zonse zimene Mulungu anacita nao.

5. Koma anauka ena a mpatuko wa Afarisi okhulupira, nati, Kuyenera kuwadula iwo, ndi kuwauza kuti asunge cilamulo ca Mose.

6. Ndipo anasonkhana atumwi ndi akuru kuti anene za mlanduwo.

7. Ndipo pamene panali mafunsano ambiri, Petro anaimirira, nati kwa iwo, Abale, mudziwa kuti poyamba Mulungu anasankha mwa inu, kuti m'kamwa mwanga amitundu amve mau a Uthenga Wabwino, nakhulupire.

8. Ndipo Mulungu, amene adziwa mtima, anawacitira umboni; nawapatsa Mzimu Woyera, monga anatipatsa ife;

9. ndipo sanalekanitsa ife ndi iwo, nayeretsa mitima yao m'cikhulupiriro.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 15