Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 13:42-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Ndipo pakuturuka iwo anapempha kuti alankhule naonso mau awa Sabata likudzalo.

43. Ndipo m'mene anthu a m'sunagoge anabalalika, Ayuda ambiri ndi akupinduka opembedza anatsata. Paulo ndi Bamaba; amene, polankhula nao, 8 anawaumiriza akhale m'cisomo ca Ambuye.

44. Ndipo Sabata linalo udasonkhana pamodzi ngati mudzi wonse kumva mau a Mulungu.

45. Koma Ayuda, pakuona makamu a anthu, anadukidwa, natsutsana nazo zolankhulidwa ndi Paulo, nacita mwano.

46. Ndipo Paulo ndi Bamaba analimbika mtima ponena, nati, 9 Kunafunika kuti mau a Mulungu ayambe alankhulidwe kwa inu. 10 Popeza muwakankha, nimudziyesera nokha osayenera moyo wosatha, taonani, titembenukira kwa amitundu.

47. Pakuti kotero anatilamulira Ambuye ndi kuti,11 Ndakuika iwe kuunika kwa amitundu,Kuti udzakhala iwe cipulumutso kufikira malekezero a dziko.

48. Ndipo pakumva ici amitundu anakondwera, nalemekeza mau a Mulungu; ndipo anakhulupira onse amene anaikidwiratu ku moyo wosatha.

49. Ndipo mau a Ambuye anabukitsidwa m'dziko lonse.

50. Koma Ayuda anakakamiza akazi opembedza ndi omveka, ndi akulu a mudziwo, 12 nawautsira cizunzo Paulo ndi Bamaba, ndipo ana wapitikitsaiwom'malire ao.

51. Koma iwo, 13 m'mene adawasansirapfumbi la ku mapazi ao anadza ku Ikoniyo,

52. Ndipo 14 akuphunzira anadzazidwa ndi cimwemwe ndi Mzimu Woyera.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 13