Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 13:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pamenepo iwo, otumidwa ndi Mzimu Woyera, anatsikira ku Selukeya; ndipo pocokerapo anapita m'ngalawa ku Kupro.

5. Ndipo pokhala ku Salami, analalikira mau a Mulungu m'masunagoge a Ayuda; ndipo anali nayenso Yohane mnyamata wao.

6. Ndipo m'mene anapitirira cisumbu conse kufikira Pafo, anapezapo munthu watsenga, mneneri wonyenga, ndiye Myuda, dzina lace Baryesu;

7. ameneyo anali ndi kazembe Sergio Paulo, ndiye munthu wanzeru. Yemweyo anaitana Barnaba ndi Saulo, nafunitsa kumva mau a Mulungu.

8. Koma Elima watsengayo (pakuti dzina lace litera posandulika) anawakaniza, nayesa kupatutsa kazembe asakhulupire.

9. Koma Saulo, ndiye Paulo, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anampenyetsetsa iye,

10. nati, Wodzala ndi cinyengo conse ndi cenjerero lonse, iwe, mwana wa mdierekezi, mdani wa cilungamo conse, kodi sudzaleka kuipsa njira zolunjika za Ambuye?

11. Ndipo tsopano, taona, dzanja la Ambuye liri pa iwe, ndipo udzakhala wakhungu wosapeoya dzuwa nthawi, Ndipo pomwepo lidamgwera khungu ndi mdima; ndipo anamukamoka oaf una wina womgwira dzanja.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 13