Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 13:36-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Pakutitu, Davine, m'mene adautumikira uphungu wa Mulungu m'mbadwo mwace mwa iye yekha, anagona tulo, naikidwa kwa makolo ace, naona cibvundi;

37. koma iye amene Mulungu anamuukitsa sanaona cibvundi.

38. Potero padziwike ndi inu amuna abale, 5 kuti mwa iye cilalikidwa kwa inu cikhululukiro ca macimo;

39. ndipo 6 mwa iye yense wokhulupira ayesedwa wolungama kumcotsera zonse zimene simunangathe kudzicotsera poyesedwa wolungama ndi cilamulo ca Mose.

40. Cifukwa cace penyerani, kuti cingadzere inu conenedwa ndi anenenwo:

41. 7 Taona ni, opeputsa inu, zizwani, kanganukani;Kuti ndigwiritsa nchito Ine masikuanu,Nchito imene simudzaikhulupira wina akakuuzani.

42. Ndipo pakuturuka iwo anapempha kuti alankhule naonso mau awa Sabata likudzalo.

43. Ndipo m'mene anthu a m'sunagoge anabalalika, Ayuda ambiri ndi akupinduka opembedza anatsata. Paulo ndi Bamaba; amene, polankhula nao, 8 anawaumiriza akhale m'cisomo ca Ambuye.

44. Ndipo Sabata linalo udasonkhana pamodzi ngati mudzi wonse kumva mau a Mulungu.

45. Koma Ayuda, pakuona makamu a anthu, anadukidwa, natsutsana nazo zolankhulidwa ndi Paulo, nacita mwano.

46. Ndipo Paulo ndi Bamaba analimbika mtima ponena, nati, 9 Kunafunika kuti mau a Mulungu ayambe alankhulidwe kwa inu. 10 Popeza muwakankha, nimudziyesera nokha osayenera moyo wosatha, taonani, titembenukira kwa amitundu.

47. Pakuti kotero anatilamulira Ambuye ndi kuti,11 Ndakuika iwe kuunika kwa amitundu,Kuti udzakhala iwe cipulumutso kufikira malekezero a dziko.

48. Ndipo pakumva ici amitundu anakondwera, nalemekeza mau a Mulungu; ndipo anakhulupira onse amene anaikidwiratu ku moyo wosatha.

49. Ndipo mau a Ambuye anabukitsidwa m'dziko lonse.

50. Koma Ayuda anakakamiza akazi opembedza ndi omveka, ndi akulu a mudziwo, 12 nawautsira cizunzo Paulo ndi Bamaba, ndipo ana wapitikitsaiwom'malire ao.

51. Koma iwo, 13 m'mene adawasansirapfumbi la ku mapazi ao anadza ku Ikoniyo,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 13