Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 13:21-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo kuyambira pamenepo anapempha mfumu; ndipo Mulungu anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, munthu wa pfuko la Benjamini, zaka makumi anai.

22. Ndipo m'mene atamcotsa iye, anawautsira Davine akhale mfumu yao; amenenso anamcitira umboni, nati, Ndapeza Davine, mwana wa Jese, munthu wa pamtima panga, amene adzacita cifuniro canga conse.

23. Wocokera mu mbeu yace Mulungu, monga mwa lonjezano, anautsira Israyeli Mpulumutsi, Yesu;

24. Yohane atalalikiratu, asanafike iye, ubatizo wa kulapa kwa anthu onse a Israyeli.

25. Ndipo pakukwaniritsa njira yace Yohane, ananena, Muyesa kuti ine ndine yani? Ine sindine iye. Koma taonani, akudza wina wonditsata ine, amene sindiyenera kummasulira nsapato za pa mapazi ace.

26. Amuna, abale, ana a mbadwa ya Abrahamu, ndi iwo mwa inu akuopa Mulungu, kwa ife atumidwa mau a cipulumutso ici.

27. Pakuti iwo akukhala m'Yerusalemu, ndi akulu ao, popeza sanamzindikira iye, ngakhale mau a aneneri owerengedwa masabata onse, anawakwaniritsa pakumtsutsa.

28. Ndipo ngakhale sanapeza cifukwa ca kumphera, anapempha Pilato kuti aphedwe.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 13