Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 11:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. nanena kuti, Munalowa kwa anthu osadulidwa, ndi kudya nao.

4. Koma Petro anayamba kuwafotokozera cilongosolere, nanena,

5. Ndinali ine m'mudzi wa Yopa ndi kupemphera; ndipo m'kukomoka ndinaona masomphenya, cotengera cirikutsika, ngati cinsaru cacikuru cogwiridwa pa ngondya zace zinai; ndi kutsika kumwamba, ndipo cinadza pali ine;

6. cimeneco ndidacipenyetsetsa ndinacilingirira, ndipo ndinaona nyama za miyendo inai za padziko ndi zirombo, ndi zokwawa, ndi mbalame za m'mlengalenga.

7. Ndipo ndinamvanso mau akunena ndi ine, Tauka Petro; ipha, nudye.

8. Koma ndinati, Iaitu, Ambuye; pakuti kanthu wamba, kapena konyansa sikanalowe m'kamwa mwanga ndi kale lonse.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 11