Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 11:24-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. cifukwa anali munthu wabwino, ndi wodzala ndi Mzimu Woyera ndi cikhulupiriro: ndipo khamu lalikuru lidaonjezeka kwa Ambuye.

25. Ndipo anaturuka kunka ku Tariso kufunafuna Saulo;

26. ndipo m'mene anampeza, anadza naye ku Antiokeya. Ndipo kunali, kuti caka conse anasonkhana pamodzi mu Mpingo, naphunzitsa anthu aunyinji; ndipo ophunzira anayamba kuchedwa Akristu ku Antiokeya.

27. Koma masiku awa aneneri anatsika ku Yerusalemu kudza ku Antiokeya.

28. Ndipo anyanamuka mmodzi wa iwo, dzina lace Agabo, nalosa mwa Mzimu, kuti padzakhala njala yaikulu pa dziko lonse lokhalamo anthu; ndiyo idadza masiku a Klaudiyo.

29. Ndipo akuphunzira, yense monga anakhoza, anatsimikiza mtima kutumiza zothandiza abale akukhala m'Yudeya;

30. iconso anacita, natumiza kwa akulu mwa dzanja la Bamaba ndi Saulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 11