Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 11:22-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo mbiri yao inamveka m'makutu a Mpingo wakukhala m'Yerusalemu; ndipo anatuma Bamaba apite kufikira ku Antiokeya;

23. ameneyo, m'mene anafika, naona cisomo ca Mulungu, anakondwa; ndipo anawandandaulira onse, kuti atsimikize mtima kukhalabe ndi Ambuye;

24. cifukwa anali munthu wabwino, ndi wodzala ndi Mzimu Woyera ndi cikhulupiriro: ndipo khamu lalikuru lidaonjezeka kwa Ambuye.

25. Ndipo anaturuka kunka ku Tariso kufunafuna Saulo;

26. ndipo m'mene anampeza, anadza naye ku Antiokeya. Ndipo kunali, kuti caka conse anasonkhana pamodzi mu Mpingo, naphunzitsa anthu aunyinji; ndipo ophunzira anayamba kuchedwa Akristu ku Antiokeya.

27. Koma masiku awa aneneri anatsika ku Yerusalemu kudza ku Antiokeya.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 11