Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 11:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma atumwi ndi abale akukhala m'Yudeya anamva kuti amitundunso adalandira mau a Mulungu.

2. Ndipo pamene Petro adakwera kudza ku Yerusalemu, iwo a kumdulidwe anatsutsana naye,

3. nanena kuti, Munalowa kwa anthu osadulidwa, ndi kudya nao.

4. Koma Petro anayamba kuwafotokozera cilongosolere, nanena,

5. Ndinali ine m'mudzi wa Yopa ndi kupemphera; ndipo m'kukomoka ndinaona masomphenya, cotengera cirikutsika, ngati cinsaru cacikuru cogwiridwa pa ngondya zace zinai; ndi kutsika kumwamba, ndipo cinadza pali ine;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 11