Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 11:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma atumwi ndi abale akukhala m'Yudeya anamva kuti amitundunso adalandira mau a Mulungu.

2. Ndipo pamene Petro adakwera kudza ku Yerusalemu, iwo a kumdulidwe anatsutsana naye,

3. nanena kuti, Munalowa kwa anthu osadulidwa, ndi kudya nao.

4. Koma Petro anayamba kuwafotokozera cilongosolere, nanena,

5. Ndinali ine m'mudzi wa Yopa ndi kupemphera; ndipo m'kukomoka ndinaona masomphenya, cotengera cirikutsika, ngati cinsaru cacikuru cogwiridwa pa ngondya zace zinai; ndi kutsika kumwamba, ndipo cinadza pali ine;

6. cimeneco ndidacipenyetsetsa ndinacilingirira, ndipo ndinaona nyama za miyendo inai za padziko ndi zirombo, ndi zokwawa, ndi mbalame za m'mlengalenga.

7. Ndipo ndinamvanso mau akunena ndi ine, Tauka Petro; ipha, nudye.

8. Koma ndinati, Iaitu, Ambuye; pakuti kanthu wamba, kapena konyansa sikanalowe m'kamwa mwanga ndi kale lonse.

9. Koma mau anayankha nthawi yaciwiri oturuka m'mwamba, Cimene Mulungu anaciyeretsa, usaciyesera cinthu wamba.

10. Ndipo ici cinacitika katatu; ndipo zinakwezekanso zonse kumwamba.

11. Ndipo taonani, pomwepo amuna atatu anaima pa khomo la nyumba m'mene munali ife, anatumidwa kwa ine ocokera ku Kaisareya.

12. Ndipo Mzimu anandiuza ndinke nao, wosasiyanitsa konse. Ndipo abale awa asanu ndi mmodzi anandiperekezanso anamuka nane; ndipo tinalowa m'nyumba ya munthuyo;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 11