Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 10:28-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. ndipo anati kwa iwo, Mudziwa inu nokha kuti sikuloledwa kwa munthu Myuda adziphatike kapena kudza kwa munthu wa mtundu wina; koma Mulungu anandionetsera ine ndisanenere ali yense ali munthu wamba kapena wonyansa;

29. cifukwa cacenso ndinadza wosakana, m'mene munatuma kundiitana. Pamenepo ndifunsa, mwandiitaniranji?

30. Ndipo Komeliyo anati, Atapita masiku anai, kufikira monga ora ili, ndinalikupemphera m'nyumba yanga pa ora lacisanu ndi cinai; ndipo taonani, padaimirira pamaso panga munthu wobvala cobvala conyezimira,

31. nati Komeliyo, lamveka pemphero lako, ndi zopereka zacifundo zako zakumbukika pamaso pa Mulungu.

32. Cifukwa cace tumiza anthu ku Yopa, akaitane Simoni amene anenedwanso Petro; amene acerezedwa m'nyumba ya Simoni wofufuta zikopa, m'mbali mwa nyanja.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 10