Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 9:23-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo iye ananena kwa onse, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wace tsiku ndi tsiku, nanditsate Ine.

24. Pakutiamene ali yense akafuna kupulumutsa moyo wace, iye adzautaya; koma amene ali yense akataya moyo wace cifukwa ca Ine, iye adzaupulumutsa uwu.

25. Pakuti munthu apindulanji, akadzilemezera dziko lonse lapansi nadzitayapo, kapena kulipapo moyo wace?

26. Pakuti amene ali yense: adzacita manyazi cifukwa ca Ine ndi mau anga, Mwana wa munthu adzacita manyazi cifukwa ca iye, pamene adzafika ndi ulemerero wace ndi wa Atate, ndi wa angelo oyera.

27. Koma Ine ndinena ndi inu zoonadi, Kuli ena a iwo akuimirira pano, amene sadzalawatu imfa, kufikira kuti adzaona Ufumu wa Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Luka 9