Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 9:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo iye anawauzitsa iwo, nalamulira kuti asanene ici kwa munthu ali yense;

22. nati, Kuyenera kuti Mwana wa munthu amve zowawa zambiri, ndi kukanidwa ndi akuru, ndi ansembe akuru, ndi alembi, ndi kuphedwa, ndi kuuka tsiku lacitatu.

23. Ndipo iye ananena kwa onse, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wace tsiku ndi tsiku, nanditsate Ine.

24. Pakutiamene ali yense akafuna kupulumutsa moyo wace, iye adzautaya; koma amene ali yense akataya moyo wace cifukwa ca Ine, iye adzaupulumutsa uwu.

Werengani mutu wathunthu Luka 9