Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 8:35-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Ndipo iwo anaturuka kukaona cimene cinacitika; ndipo anadza kwa Yesu, nampeza munthuyo, amene ziwanda zinaturuka mwa iye, alikukhala pansi ku mapazi ace a Yesu wobvala ndi wa nzeru zace; ndipo iwo anaopa.

36. Ndipo amene anaona anawauza iwo maciritsidwe ace a wogwidwa ciwandayo.

37. Ndipo anthu aunyinji onse a dziko la Agerasa Ioyandikira anamfunsa iye acoke kwa iwo; cifukwa anagwidwa ndi mantha akuru. Ndipo iye analowa m'ngalawa, nabwerera.

Werengani mutu wathunthu Luka 8