Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 8:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, katapita kamphindi anayendayenda kumizinda ndi kumidzi, kulalikira ndi kuwauza U thenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu, ndi pamodzi naye khumi ndi awiriwo,

2. ndi akazi ena amene anaciritsidwa mizimu yoipa ndi nthenda zao, ndiwo, Mariya wonenedwa Magadalene, amene ziwanda zisanu ndi ziwiri zinaturuka mwa iye,

3. ndi Yohana, mkazi wace wa Kuza kapitao wa Herode, ndi Susana, ndi ena ambiri, amene anawatumikira ndi eumacao.

4. Ndipo pamene khamu lalikuru la anthu linasonkhana, ndi anthu a ku midzi yonse anafika kwa iye, anati mwa fanizo:

5. Anaturuka wofesa kukafesa mbeu zace; ndipo m'kufesa kwace zina zinagwa m'mbali mwa njira; ndipo zinapondedwa, ndi mbalame za m'mlengalenga zinatha kuzidya.

6. Ndipo zina zinagwa pathanthwe; ndipo pakumera zinatofa msanga, cifukwa zinalibe mnyontho.

7. Ndipo zina zinagwa pakati pa minga; ndi mingayo inapuka pamodzi nazo, nizitsamwitsa.

8. Ndipo zina zinagwa pa nthaka yokoma, ndipo zinamera, ndi kupatsa zipatso zamakumikhumi. Pakunena iye izi anapfuula, iye amene ali ndi makutu akumva amve.

Werengani mutu wathunthu Luka 8