Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 7:39-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Koma Mfarisi, amene adamuitana iye, pakuona, ananena mwa yekha, nati, Akadakhala mneneri uyu akadazindikira ali yani, ndi wotani mkaziyo womkhudza iye, cifukwa ali wocimwa.

40. Ndipo Yesu anayankha nati kwa iye, Simoni, ndiri ndi kanthu kakunena kwa iwe. Ndipo iye anabvomera, Mphunzitsi, nenani.

41. Munthu wokongoletsa ndalama anali nao amangawa awiri; mmodziyo anali ndi mangawa ace a marupiya mazana asanu, koma mnzace makumi asanu.

42. Popeza analibe cobwezera iwo, anawakhululukira onse awiri. Cotero, ndani wa iwo adzaposa kumkonda?

43. Simoni anayankha, nati, Ndiyesa kuti, iye amene anamkhululukira zoposa,

44. Ndipo anati kwa iye, Waweruza bwino. Ndipo m'mene iye anaceukira kwa mkaziyo, anati kwa Simoni, Upenya mkazi ameneyu kodi? Ndinalowa m'nyumba yako, sunandipatsa madzi akusambitsa mapazi anga; koma uyu anakonkha mapazi anga ndi misozi, nawapukuta ndi tsitsi lace.

45. Sunandipatsa mpsompsono wa cibwenzi; koma uyu sanaleka kupsompsonetsa mapazi anga, cilowere muno Ine.

Werengani mutu wathunthu Luka 7