Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 7:35-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Ndipo nzeru iyesedwa yolungama ndi ana ace onse.

36. Ndipo mmodzi wa Afarisi anamuitana iye kuti akadye naye. Ndipo analowa m'nyumba ya Mfarisi, naseama pacakudya.

37. Ndipo onani, mkazi wocimwa, amene anali m'mudzimo; ndipo pakudziwa kuti Yesu analikuseama pacakudya m'nyumba ya Mfarisi, anatenga nsupa yaalabastero ya mafuta onunkhira bwino,

38. naimirira kumbuyo, pa mapazi ace, nalira, nayamba kukhathamiza mapazi ace ndi misozi, nawapukuta ndi tsitsi la mutu wace, nampsompsonetsa mapazi ace, nawadzoza ndi mafuta onunkhira bwino.

39. Koma Mfarisi, amene adamuitana iye, pakuona, ananena mwa yekha, nati, Akadakhala mneneri uyu akadazindikira ali yani, ndi wotani mkaziyo womkhudza iye, cifukwa ali wocimwa.

40. Ndipo Yesu anayankha nati kwa iye, Simoni, ndiri ndi kanthu kakunena kwa iwe. Ndipo iye anabvomera, Mphunzitsi, nenani.

41. Munthu wokongoletsa ndalama anali nao amangawa awiri; mmodziyo anali ndi mangawa ace a marupiya mazana asanu, koma mnzace makumi asanu.

42. Popeza analibe cobwezera iwo, anawakhululukira onse awiri. Cotero, ndani wa iwo adzaposa kumkonda?

43. Simoni anayankha, nati, Ndiyesa kuti, iye amene anamkhululukira zoposa,

44. Ndipo anati kwa iye, Waweruza bwino. Ndipo m'mene iye anaceukira kwa mkaziyo, anati kwa Simoni, Upenya mkazi ameneyu kodi? Ndinalowa m'nyumba yako, sunandipatsa madzi akusambitsa mapazi anga; koma uyu anakonkha mapazi anga ndi misozi, nawapukuta ndi tsitsi lace.

45. Sunandipatsa mpsompsono wa cibwenzi; koma uyu sanaleka kupsompsonetsa mapazi anga, cilowere muno Ine.

46. Sunandidzoza mutu wanga ndi mafuta; koma nyu anadzoza mapazi anga ndimafuta onunkhira bwmo.

47. Cifukwa cace, ndinena kwa iwe, Macimo ace, ndiwo ambiri, akhululukidwa; cifukwa anakonda kwambiri; koma munthu amene anamkhululukira pang'ono, iye akonda pang'ono.

48. Ndipo anati kwa mkazi, Macimo ako akhululukidwa.

49. Ndipo iwo akuseama naye pacakudya anayamba kunena mwa okha, Uyu ndani amene akhululukiranso macimo?

50. Ndipo Iyeanati kwa mkaziyo, Cikhulupiriro cako cakupulumutsa iwe; muka ndi mtendere.

Werengani mutu wathunthu Luka 7