Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 7:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo ophunzira a Yohane anamuuza iye zonsezi.

19. Ndipo Yohane anaitana awiri a ophunzira ace, nawatuma kwa Ambuye, nanena, Kodi ndinu wakudzayo, kapena tiyang'anire wina?

20. Ndipo pakufika kwa iye anthu awo, anati, Yohane Mbatizi watituma ife kwa Inu, kuti, Kodi ndinu wakudzayo, kapena tiyang'anire wina?

21. Nthawi yomweyo iye anaciritsa anthu ambiri nthenda zao, ndi zobvuta, ndi mizimu yoipa; napenyetsanso anthu akhungu ambiri.

Werengani mutu wathunthu Luka 7