Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 6:38-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. 6 Patsani, ndipo kudzapatsidwa kwa inu; muyeso wabwino, wotsendereka, wokucumuka, wosefukira, anthu adzakupatsani m'manja mwanu. Pakuti 7 kudzayesedwa kwa inu ndi muyeso womwewo muyesa nao inu.

39. Ndipo iye ananenanso nao fanizo, 8 Kodi munthu wakhungu angathe kutsogolera mnzace wakhungu? kodi sadzagwa onse awiri m'mbuna?

40. 9 Wophunzira saposa mphunzitsi wace; koma yense, m'mene atakonzedwa mtima, adzafanana ndi mphunzitsi wace.

41. Ndipo uyang'aniranji kacitsotso kali m'diso la mbale wako, koma mtanda wa m'diso la iwe mwini suuzindikira?

42. 10 Kapena ungathe bwanji kunena kwa mbale wako, Mbale iwe, leka ndicotse kacitsotso kali m'diso lako, wosayang'anira iwe mwini mtanda uli m'diso lako? Wonyenga iwe! thanga wacotsa mtandawo m'diso lako, ndipo pomwepo udzayang'anitsa bwino kucotsa kacitsotso ka m'diso la mbale wako.

43. Pakuti 11 palibe mtengo wabwino wakupatsa zipatso zobvunda; kapenanso mtengo woipa wakupatsa zipatso zabwino,

Werengani mutu wathunthu Luka 6