Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 6:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Tsoka inu, pamene anthu onse adzanenera inu zabwino! pakuti makolo ao anawatero momwemo ananeri onama.

27. Koma ndinena kwa inu akumva, Kondanani nao adani anu; citirani zabwino iwo akuda inu,

28. dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akucitira inu cipongwe.

29. Iye amene akupanda iwe pa tsaya limodzi umpatsenso linzace; ndi iye amene alanda copfunda cako, usamkanize malaya ako.

30. Munthu ali yense akakupempha kanthu, umpatse; ndi iye amene alanda zako, usazipemphanso.

31. Ndipo monga mufuna inu kuti anthu adzakucitirani inu, muwacitire iwo motero inu momwe.

Werengani mutu wathunthu Luka 6