Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 6:23-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Kondwerani tsiku lomweli, tumphani ndi cimwemwe; pakuti onani, mphotho zanu nzazikuru Kumwamba; pakuti makolo ao anawacitira aneneri zonga zomwezo.

24. Koma tsoka inu eni cuma! cifukwa mwalandira cisangalatso canu.

25. Tsoka inu okhuta tsopano! cifukwa mudzamva njala, Tsoka inu, akuseka tsopano! cifukwa mudzacita maliro ndi kulira misozi.

26. Tsoka inu, pamene anthu onse adzanenera inu zabwino! pakuti makolo ao anawatero momwemo ananeri onama.

27. Koma ndinena kwa inu akumva, Kondanani nao adani anu; citirani zabwino iwo akuda inu,

28. dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akucitira inu cipongwe.

29. Iye amene akupanda iwe pa tsaya limodzi umpatsenso linzace; ndi iye amene alanda copfunda cako, usamkanize malaya ako.

30. Munthu ali yense akakupempha kanthu, umpatse; ndi iye amene alanda zako, usazipemphanso.

31. Ndipo monga mufuna inu kuti anthu adzakucitirani inu, muwacitire iwo motero inu momwe.

32. Ndipo 1 ngati muwakonda iwo akukondana ndinu, mudzalandira ciyamiko cotani? pakuti ocimwa omwe akonda iwo akukondana nao.

33. Ndipo ngati muwacitira zabwino iwo amene akucitirani, inu zabwino, mudzalandira ciyamiko cotani? pakuti anthu ocimwa omwe amacita comweco.

34. Ndipo 2 ngati mukongoletsa kanthu kwa iwo amene muyembekeza kulandiranso, mudzalandira ciyamiko cotani? pakuti inde anthu ocimwa amakongoletsa kwa ocimwa anzao, kuti alandirenso momwemo.

35. Koma 3 takondanani nao adani anu, ndi kuwacitira zabwino, ndipo kongoletsani osayembekeza kanthu konse, ndipo mphotho yanu idzakhala yaikuru, ndipo 4 inu mudzakhala ana a Wamkurukuruyo; cifukwa iye acitira zokoma anthu osayamika ndi oipa.

36. Khalani inu acifundo monga Atate wanu ali wacifundo. Ndipo musamaweruza, ndipo simudzaweruzidwa.

Werengani mutu wathunthu Luka 6