Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 6:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. ndi khamu lonse lija linafuna kumkhudza iye; cifukwa munaturuka mphamvu mwa iye, niciritsa onsewa.

20. Ndipo iye anakweza maso ace kwa ophunzira ace, nanena, Odala osauka inu; cifukwa uli wanu ufumu wa Mulungu.

21. Odala inu akumva njala tsopano; cifukwa mudzakhuta. Odala inu akulira tsopano; cifukwa mudzaseka.

22. Odala inu, pamene anthu adzada inu, nadzapatula inu, nadzatonza inu, nadzalitaya dzina lanu monga loipa, cifukwa ca Mwana wa munthu.

23. Kondwerani tsiku lomweli, tumphani ndi cimwemwe; pakuti onani, mphotho zanu nzazikuru Kumwamba; pakuti makolo ao anawacitira aneneri zonga zomwezo.

24. Koma tsoka inu eni cuma! cifukwa mwalandira cisangalatso canu.

Werengani mutu wathunthu Luka 6