Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 5:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali, pakumkanikiza khamu la anthu, kudzamva mau a Mulungu, iye analikuimirira m'mbali mwa nyanja ya Genesarete;

2. ndipo anaona ngalawa ziwiri zinakhala m'mbali mwa nyanja; koma asodzi a nsomba adaturuka m'menemo, nalikutsuka makoka ao.

3. Ndipo iye analowa m'ngalawa imodzi, ndiyo yace ya Simoni, nampempha iye akankhe pang'ono. Ndipo anakhala pansi m'menemo, naphunzitsa m'ngalawa makamuwo a anthu.

4. Ndipo pamene iye analeka kulankhula, anati kwa Simoni, Kankhira kwa kuya, nimuponye makoka anu kukasodza.

Werengani mutu wathunthu Luka 5