Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 4:20-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo m'mene iye anapinda bukulo, nalipereka kwa mnyamata, anakhala pansi; ndipo maso ao a anthu onse m'sunagogemo anamyang'anitsa iye.

21. Ndipo anayamba kunena kwa iwo, kuti, Lero lembo ili lakwanitsidwa m'makutu anu.

22. Ndipo onse anamcitira iye umboni nazizwa ndi mau a cisomo akuturuka m'kamwa mwace; nanena, Kodi uyu si mwana wa Yosefe?

Werengani mutu wathunthu Luka 4